National Anthem of Malawi - Mlungu Dalitsani Malaŵi (Instrumental)

3 years ago
22

"Mlungu dalitsani Malaŵi" (English: "O God bless our land of Malawi") is the national anthem of Malawi. It was composed by Michael-Fredrick Paul Sauka, who also wrote the lyrics.

(Chichewa Lyrics / Cheŵa)
Mlungu dalitsani Malaŵi,
Mumsunge m'mtendere.
Gonjetsani adani onse,
Njala, nthenda, nsanje.
Lunzitsani mitima yathu,
Kuti tisaope.
Mdalitse Mtsogoleri nafe,
Ndi Mayi Malaŵi.

Malaŵi ndziko lokongola,
La chonde ndi ufulu,
Nyanja ndi mphepo ya m'mapiri,
Ndithudi tadala.
Zigwa, mapiri, nthaka, dzinthu,
N'mphatso zaulere.
Nkhalango, madambo abwino.
Ngwokoma Malaŵi.

O Ufulu tigwirizane,
Kukweza Malaŵi.
Ndi chikondi, khama, kumvera,
Timutumikire.
Pa nkhondo nkana pa mtendere,
Cholinga n'chimodzi.
Mayi, bambo, tidzipereke,
Pokweza Malaŵi.

Hymne National du Malawi / Hino Nacional do Malawi / Himno Nacional de Malawi / Nationalhymne Malawi /

Loading comments...